< Masalimo 91 >

1 Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
Deɛ ɔte Ɔsorosoroni no hintabea bɛhome wɔ Otumfoɔ no nwunu mu.
2 Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.”
Mɛse Awurade sɛ, “Woyɛ me dwanekɔbea ne mʼabankɛseɛ, me Onyankopɔn a mewɔ wo mu ahotosoɔ.”
3 Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa;
Ampa ara, ɔbɛgye wo afiri fidisumfoɔ afidie mu ne owuyadeɛ mu.
4 Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
Ɔde ne ntakra bɛkata wo so; na ne ntaban ase na wobɛnya dwanekɔbea; ne nokorɛ bɛyɛ wo banbɔ ne wo kyɛm.
5 Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,
Worensuro anadwo mu ahunahuna, anaa bɛmma a ɛtu awia,
6 kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
anaa owuyadeɛ a ɛba esum mu, anaa ɔyaredɔm a ɛsɛe owigyinaeɛ.
7 Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
Apem bɛtotɔ wo nkyɛn mu, na ɔpedu bɛtotɔ wo nifa, nanso, wo deɛ, ɛrenka wo.
8 Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
Wʼani nko ara na wode bɛhwɛ na woahunu nnebɔneyɛfoɔ asotwe.
9 Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
Sɛ wode Ɔsorosoroni no yɛ wo tenabea, mpo Awurade a ɔyɛ me dwanekɔbea no a,
10 Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
ɔhaw biara remma wo so, na amanehunu biara remmɛn wo ntomadan.
11 Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
Ɛfiri sɛ ɔbɛhyɛ nʼabɔfoɔ a wɔhwɛ wo so no abɛbɔ wo ho ban wʼakwan nyinaa mu;
12 ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
wɔde wɔn nsa bɛpagya wo, na wo nan rensunti ɔboɔ.
13 Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
Wobɛtiatia agyata ne aprammire so, wobɛnante gyataburuwa ne ɔtweaseɛ so.
14 “Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
Awurade ka sɛ, “Esiane sɛ ɔdɔ me enti, mɛgye no; mɛbɔ ne ho ban, ɛfiri sɛ ɔnim me din.
15 Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
Ɔbɛfrɛ me, na mɛgye ne so; mɛka ne ho wɔ amanehunu mu, mɛgye no, na mahyɛ no animuonyam.
16 Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”
Mɛma nkwa nna a ɛware amee no na makyerɛ no me nkwagyeɛ.”

< Masalimo 91 >