< Masalimo 91 >
1 Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
I mpimoneñe am-pipalira’ i Andindimoneñeiy, ty hitoetse añ’alo’ i El-Sadai ao,
2 Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.”
Hanoako ty hoe t’Iehovà: Ty fiampirako, ty rova fitsolohako, i Andrianañahare fiatoakoy.
3 Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa;
Ie ty mpañaha azo boak’ am-bitsom-pamandri-boroñe ao, naho boak’ amy biloka mahahomakey.
4 Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
Haholonkolo’e am-bolon-ela’e ao irehe, ambane’ o ela’eo ty hipalira’o; fikalan-defo naho fikala-meso ty hatò’e.
5 Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,
Tsy hahahembañ’ azo ty hetraketrak’ an-kaleñe, ndra ty ana-pale mihirirìñe an-tariñandroke.
6 kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
Ndra ty kiria mitingañe añ’ieñe ao ndra ty angorosy mamotsake naho antoandro.
7 Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
Arivo ty mete hikorovok’ añ’ ila’o eo, le rai-ale ty am-pitàn-kavana’o eo, f’ie tsy hitotok’ azo.
8 Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
O fihaino’oo avao ro hisamba, hahaisake ty fandilovañe o lo-tserekeo.
9 Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
Amy te Iehovà, fitsolohako, i Andindimoneñey, ty nanoe’o fimoneñañe,
10 Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
Tsy hidoiñe ama’o ty hankàñe, tsy hitotofan-angorosy ty akiba’o,
11 Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
Fa hafanto’e ama’o o anjeli’eo, hañambeñe azo amo lia’o iabio;
12 ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
hañotrotroa’e am-pità’e ao, tsy mone hadasi’o ami’ty vato ty fandia’o.
13 Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
Ho lià’o ty liona naho ty fandrefeala; ho hitsakitsahe’o ambanem-pandia’o eo ty liona-tora’e naho i mereñey.
14 “Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
Kanao ifahara’e koko, ho hahako, havotrako an-kaboañe ey amy te fohi’e ty añarako.
15 Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
Ho kanjie’e, le ho toiñeko; hindrezako te am-poheke, ho votsorako vaho ho tolorako asiñe.
16 Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”
Heneñeko halava’ havelon-dre; vaho hampahaoniñeko aze ty fandrombahako.