< Masalimo 91 >
1 Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
Ti što prebivaš pod zaštitom Višnjega, što počivaš u sjeni Svemogućega,
2 Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.”
reci Jahvi: “Zaklone moj! Utvrdo moja! Bože moj u koga se uzdam!”
3 Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa;
Jer on će te osloboditi od zamke ptičarske, od kuge pogubne.
4 Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
Svojim će te krilima zaštititi i pod njegova ćeš se krila skloniti: Vjernost je njegova štit i obrana!
5 Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,
Nećeš se bojati strašila noćnoga ni strelice što leti danju,
6 kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
ni kuge što se šulja kroz tmine, ni pošasti što hara o podne.
7 Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
Pa nek' padaju tisuće kraj tebe, deseci tisuća s desne tvoje, tebi se neće primaći!
8 Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
Tek što okom pogledaš, već ćeš vidjeti plaću grešnika.
9 Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
Jer Jahve je zaklon tvoj, Višnjega odabra sebi za okrilje.
10 Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
Neće te snaći nesreća, nevolja se neće prikučiti šatoru tvojemu.
11 Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
Jer anđelima svojim zapovjedi da te čuvaju na svim putima tvojim.
12 ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
Na rukama će te nositi da se ne spotakneš o kamen.
13 Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
Nogom ćeš gaziti lava i ljuticu, zgazit ćeš lavića i zmiju.
14 “Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
Izbavit ću ga jer me ljubi, zakrilit ga jer poznaje ime moje.
15 Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
Zazvat će me, a ja ću ga uslišiti, s njim ću biti u nevolji, spasit ću ga i proslaviti.
16 Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”
Nasitit ću ga danima mnogim, pokazat' mu spasenje svoje.”