< Masalimo 90 >
1 Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
Молитва Мойсея, чоловіка Божого. Владико, Ти був пристановищем нашим з роду в рід.
2 Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
Перш ніж народилися гори й Ти утворив землю і всесвіт, від віку й до віку Ти – Бог.
3 Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
Ти повертаєш людину назад у порох і кажеш: «Поверніться назад, сини людські!»
4 Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
Адже тисяча років в очах Твоїх, немов день вчорашній, що минає, як сторожа вночі.
5 Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
Потоком Ти несеш людей, немов сон минули вони; як трава, що вранці сходить,
6 ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
вранці цвіте й рясніє, а ввечері в’яне й засихає.
7 Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
Ми щезаємо у гніві Твоєму, і через лють Твою ми збентежені.
8 Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
Ти поклав наші беззаконня перед Собою, наші приховані [гріхи вивів] на світло Твого обличчя.
9 Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
Бо всі дні наші проходять у люті Твоїй; роки наші згасають, немов стогін.
10 Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
Днів наших – сімдесят років, а якщо є сила, то вісімдесят років, і найкраще в них [забирає] праця й смуток; вони минають швидко, і ми відлітаємо.
11 Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
Хто знає силу гніву Твого? Страх перед Тобою, [настільки великий], як і лють Твоя.
12 Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
Навчи нас так лічити дні наші, щоб ми набули мудре серце.
13 Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
Повернися ж, Господи, доки так буде? Змилуйся над рабами Твоїми!
14 Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
Насичуй нас милістю Твоєю вранці, тоді ми веселитися й радіти будемо по всі дні наші.
15 Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
Дай нам порадіти за ті дні, коли Ти упокорював нас, за ті роки, коли ми бачили лихо.
16 Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
Нехай з’явиться Твоє діло рабам Твоїм, і велич Твоя – синам їхнім.
17 Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.
І нехай перебуватиме прихильність Володаря, Бога нашого, на нас. Справу рук наших утверди для нас, справу рук наших зміцни нам.