< Masalimo 90 >

1 Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
Molitev Mojzesova, moža Božjega: O Gospod, ti si nam bil prebivališče od roda do roda,
2 Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
Ko niso bile še rojene gore, in nisi bil naredil zemlje in vesoljnega sveta, dà od vekomaj do vekomaj Bog si tí mogočni.
3 Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
Pripraviš človeka tako daleč, da je potrt, govoreč: "Povrnite se, sinovi človeški!"
4 Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
Ker če tisoč lét preide, v tvojih očéh so, kakor včerajšnji dan, in straža nočna.
5 Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
S povodnjo jih pokončaš, spanje so, zjutraj so kakor seno, ki mine.
6 ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
Zjutraj, ko se je razcvelo, mine; pokosi in posuši se zvečer.
7 Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
Ker ginemo od jeze tvoje, in srd tvoj nas plaši:
8 Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
Pred oči si staviš krivice naše, skrivnosti naše v luč svojega obličja.
9 Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
Ker vsi dnevi naši ginejo v srdu tvojem; leta naša nam tekó misli enaka.
10 Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
V samih dnevih lét naših je sedemdeset let; ali (ako smo prav krepki) osemdeset let; celo kar je v njih najboljše, polno je truda in težav; ko to hitro mine, odletimo.
11 Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
Kdo spozna jeze tvoje moč, ali srdú tvojega po strahu tvojem?
12 Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
Šteti nas úči naše dni tako, da dobimo srce modro.
13 Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
Vrni se, Gospod! Doklej! in kesaj se zavoljo hlapcev svojih.
14 Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
Nasiti nas vsako jutro z milostjo svojo, da pojemo in se radujemo vse svoje dni.
15 Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
Razveséli nas, kakor si nas ponižaval mnogo dnî; mnogo let smo izkušali húdo.
16 Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
Očitno bodi hlapcem tvojim delo tvoje, in lepota tvoja med njih sinovi.
17 Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.
Na strani nam bodi prijetnost Gospoda, Boga našega, in delo naših rok podpiraj v nas; sámo delo, pravim, naših rok podpiraj.

< Masalimo 90 >