< Masalimo 90 >

1 Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
Nkosi, wena ubuyindawo yethu yokuhlala kusizukulwana lesizukulwana.
2 Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
Zingakazalwa intaba, kumbe uveze umhlaba lelizwe, ngitsho kusukela ephakadeni kuze kube sephakadeni wena unguNkulunkulu.
3 Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
Uyambuyisela umuntu encithakalweni, uthi: Buyelani, bantwana babantu.
4 Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
Ngoba iminyaka eyinkulungwane emehlweni akho injengelanga lezolo selidlulile, lanjengomlindo ebusuku.
5 Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
Uyabakhukhula, banjengobuthongo, ekuseni banjengotshani obuhlumayo.
6 ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
Ekuseni buyakhahlela, bukhule, ntambama buyasikwa, bubune.
7 Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
Ngoba siqedwa yikuthukuthela kwakho, langolaka lwakho sibhujiswe.
8 Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
Ubekile iziphambeko zethu phambi kwakho, izono zethu ezifihlakeleyo ekukhanyeni kobuso bakho.
9 Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
Ngoba insuku zethu zonke ziyedlula elakeni lwakho; sichitha iminyaka yethu njengokubeka iphika.
10 Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
Insuku zeminyaka yethu, kuleminyaka engamatshumi ayisikhombisa kuzo; njalo uba ngenxa yamandla zingamatshumi ayisificaminwembili, kanti ukuzigqaja kwayo kuyinhlupheko losizi, ngoba aphangisa aqunywe, sibe sesiphapha sinyamalale.
11 Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
Ngubani owaziyo amandla okuthukuthela kwakho? Lanjengokwesabeka kwakho lunjalo ulaka lwakho.
12 Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
Ngokunjalo sifundise ukubala insuku zethu, ukuze sizuze inhliziyo yenhlakanipho.
13 Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
Phenduka, Nkosi! Koze kube nini? Hawukela izinceku zakho.
14 Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
Sisuthise ekuseni ngomusa wakho, ukuze sithabe sijabule insuku zethu zonke.
15 Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
Sithokozise njengokwensuku owasihlupha ngazo, iminyaka esabona okubi kuyo.
16 Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
Umsebenzi wakho kawubonakale ezincekwini zakho, lenkazimulo yakho ebantwaneni bazo.
17 Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.
Ubuhle beNkosi, uNkulunkulu wethu, kabube phezu kwethu; uqinise umsebenzi wezandla zethu kithi, yebo, umsebenzi wezandla zethu uwuqinise.

< Masalimo 90 >