< Masalimo 90 >

1 Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
Oratio Moysi hominis Dei. Domine, refugium factus es nobis: a generatione in generationem.
2 Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
Priusquam montes fierent, aut formaretur terra, et orbis: a saeculo et usque in saeculum tu es Deus.
3 Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
Ne avertas hominem in humilitatem: et dixisti: Convertimini filii hominum.
4 Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
Quoniam mille anni ante oculos tuos, tamquam dies hesterna, quae praeteriit, Et custodia in nocte,
5 Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
quae pro nihilo habentur, eorum anni erunt.
6 ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
Mane sicut herba transeat, mane floreat, et transeat: vespere decidat, induret, et arescat.
7 Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
Quia defecimus in ira tua, et in furore tuo turbati sumus.
8 Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
Posuisti iniquitates nostras in conspectu tuo: saeculum nostrum in illuminatione vultus tui.
9 Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
Quoniam omnes dies nostri defecerunt: et in ira tua defecimus. Anni nostri sicut aranea meditabuntur:
10 Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
dies annorum nostrorum in ipsis, septuaginta anni. Si autem in potentatibus octoginta anni: et amplius eorum, labor et dolor. Quoniam supervenit mansuetudo: et corripiemur.
11 Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
Quis novit potestatem irae tuae: et prae timore tuo iram tuam
12 Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
dinumerare? Dexteram tuam sic notam fac: et eruditos corde in sapientia.
13 Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
Convertere Domine usquequo? et deprecabilis esto super servos tuos.
14 Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
Repleti sumus mane misericordia tua: exultavimus, et delectati sumus omnibus diebus nostris.
15 Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
Laetati sumus pro diebus, quibus nos humiliasti: annis, quibus vidimus mala.
16 Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
Respice in servos tuos, et in opera tua: et dirige filios eorum.
17 Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.
Et sit splendor Domini Dei nostri super nos, et opera manuum nostrarum dirige super nos: et opus manuum nostrarum dirige.

< Masalimo 90 >