< Masalimo 90 >
1 Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
BOOK IV A Prayer of Moses the man of God. Lord, Thou hast been our dwelling-place in all generations.
2 Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
Before the mountains were brought forth, or ever Thou hadst formed the earth and the world, even from everlasting to everlasting, Thou art God.
3 Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
Thou turnest man to contrition; and sayest: 'Return, ye children of men.'
4 Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
For a thousand years in Thy sight are but as yesterday when it is past, and as a watch in the night.
5 Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
Thou carriest them away as with a flood; they are as a sleep; in the morning they are like grass which groweth up.
6 ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
In the morning it flourisheth, and groweth up; in the evening it is cut down, and withereth.
7 Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
For we are consumed in Thine anger, and by Thy wrath are we hurried away.
8 Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
Thou hast set our iniquities before Thee, our secret sins in the light of Thy countenance.
9 Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
For all our days are passed away in Thy wrath; we bring our years to an end as a tale that is told.
10 Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
The days of our years are threescore years and ten, or even by reason of strength fourscore years; yet is their pride but travail and vanity; for it is speedily gone, and we fly away.
11 Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
Who knoweth the power of Thine anger, and Thy wrath according to the fear that is due unto Thee?
12 Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
So teach us to number our days, that we may get us a heart of wisdom.
13 Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
Return, O LORD; how long? And let it repent Thee concerning Thy servants.
14 Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
O satisfy us in the morning with Thy mercy; that we may rejoice and be glad all our days.
15 Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
Make us glad according to the days wherein Thou hast afflicted us, according to the years wherein we have seen evil.
16 Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
Let Thy work appear unto Thy servants, and Thy glory upon their children.
17 Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.
And let the graciousness of the Lord our God be upon us; establish Thou also upon us the work of our hands; yea, the work of our hands establish Thou it.