< Masalimo 90 >

1 Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
A Prayer of Moses the man of God. Lord, thou hast been our refuge in all generations.
2 Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
Before the mountains existed, and [before] the earth and the world were formed, even from age to age, Thou art.
3 Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
Turn not man back to [his] low place, whereas thou saidst, Return, ye sons of men?
4 Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
For a thousand years in thy sight are as the yesterday which is past, and as a watch in the night.
5 Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
Years shall be vanity to them: let the morning pass away as grass.
6 ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
In the morning let it flower, and pass away: in the evening let it droop, let it be withered and dried up.
7 Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
For we have perished in thine anger, and in thy wrath we have been troubled.
8 Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
Thou hast set our transgressions before thee: our age is in the light of thy countenance.
9 Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
For all our days are gone, and we have passed away in thy wrath: our years have spun out their tale as a spider.
10 Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
[As for] the days of our years, in them are seventy years; and if [men should be] in strength, eighty years: and the greater part of them would be labour and trouble; for weakness overtakes us, and we shall be chastened.
11 Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
Who knows the power of thy wrath?
12 Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
and [who knows how] to number [his days] because of the fear of thy wrath? So manifest thy right hand, and those that are instructed in wisdom in the heart.
13 Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
Return, O Lord, how long? and be intreated concerning thy servants.
14 Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
We have been satisfied in the morning with thy mercy; and we did exult and rejoice:
15 Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
let us rejoice in all our days, in return for the days wherein thou didst afflict us, the years wherein we saw evil.
16 Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
And look upon thy servants, and upon thy works; and guide their children.
17 Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.
And let the brightness of the Lord our God be upon us: and do thou direct for us the works of our hands.

< Masalimo 90 >