< Masalimo 9 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
למנצח עלמות לבן מזמור לדוד אודה יהוה בכל לבי אספרה כל נפלאותיך׃
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
אשמחה ואעלצה בך אזמרה שמך עליון׃
3 Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
בשוב אויבי אחור יכשלו ויאבדו מפניך׃
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
כי עשית משפטי ודיני ישבת לכסא שופט צדק׃
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
גערת גוים אבדת רשע שמם מחית לעולם ועד׃
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
האויב תמו חרבות לנצח וערים נתשת אבד זכרם המה׃
7 Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
ויהוה לעולם ישב כונן למשפט כסאו׃
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
והוא ישפט תבל בצדק ידין לאמים במישרים׃
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
ויהי יהוה משגב לדך משגב לעתות בצרה׃
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
ויבטחו בך יודעי שמך כי לא עזבת דרשיך יהוה׃
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
זמרו ליהוה ישב ציון הגידו בעמים עלילותיו׃
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
כי דרש דמים אותם זכר לא שכח צעקת עניים׃
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
חננני יהוה ראה עניי משנאי מרוממי משערי מות׃
14 kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
למען אספרה כל תהלתיך בשערי בת ציון אגילה בישועתך׃
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
טבעו גוים בשחת עשו ברשת זו טמנו נלכדה רגלם׃
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
נודע יהוה משפט עשה בפעל כפיו נוקש רשע הגיון סלה׃
17 Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
ישובו רשעים לשאולה כל גוים שכחי אלהים׃ (Sheol h7585)
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
כי לא לנצח ישכח אביון תקות ענוים תאבד לעד׃
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
קומה יהוה אל יעז אנוש ישפטו גוים על פניך׃
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)
שיתה יהוה מורה להם ידעו גוים אנוש המה סלה׃

< Masalimo 9 >