< Masalimo 9 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
Veisuunjohtajalle; veisataan kuin: "Kuole pojan puolesta"; Daavidin virsi. Minä ylistän Herraa kaikesta sydämestäni, ilmoitan kaikki sinun ihmetyösi.
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
Minä iloitsen ja riemuitsen sinussa, veisaan sinun nimesi kiitosta, sinä Korkein.
3 Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
Sillä minun viholliseni peräytyivät, kaatuivat maahan ja hukkuivat sinun kasvojesi edessä.
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
Sinä hankit minulle oikeuden ja ajoit minun asiani, sinä istuit valtaistuimelle, sinä vanhurskas tuomari.
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
Sinä nuhtelit pakanoita, tuhosit jumalattomat; sinä pyyhit pois heidän nimensä iäksi ja ainiaaksi.
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
Viholliset ovat tuhotut, ikuisiksi raunioiksi tulleet; kaupungit sinä kukistit, heidän muistonsa on kadonnut.
7 Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
Mutta Herra hallitsee iankaikkisesti; hän on pystyttänyt istuimensa tuomitaksensa.
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
Hän tuomitsee maanpiirin vanhurskaasti, vallitsee kansoja oikeuden mukaan.
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
Niin Herra on sorretun linna, linna ahdingon aikoina.
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
Ja sinuun turvaavat ne, jotka sinun nimesi tuntevat; sillä sinä et hylkää niitä, jotka sinua etsivät, Herra.
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
Veisatkaa kiitosta Herralle, joka Siionissa asuu, julistakaa kansojen keskuudessa hänen suuria tekojaan.
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
Sillä hän, verenkostaja, muistaa heitä eikä unhota kurjain huutoa.
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
Armahda minua, Herra, katso, kuinka minun vihamieheni minua vaivaavat, sinä, joka nostat minut kuoleman porteista,
14 kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
että minä julistaisin kaikki sinun ylistettävät tekosi, tytär Siionin porteissa, riemuitsisin sinun avustasi.
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
Pakanat ovat vajonneet kaivamaansa hautaan; heidän jalkansa takertui verkkoon, jonka he virittivät.
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
Herra on tehnyt itsensä tunnetuksi, on pitänyt tuomiot, kietonut jumalattoman hänen kättensä tekoihin. -Kanteleen välisoitto. (Sela)
17 Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
Jumalattomat peräytyvät tuonelaan, kaikki pakanat, jotka unhottavat Jumalan. (Sheol h7585)
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
Sillä ei köyhää unhoteta iäksi, eikä kurjien toivo huku ainiaaksi.
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
Nouse, Herra, älä salli ihmisten uhitella. Tuomittakoon pakanat sinun kasvojesi edessä.
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)
Saata, Herra, heidät pelkoon. Tietäkööt pakanat olevansa vain ihmisiä. (Sela)

< Masalimo 9 >