< Masalimo 9 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
For the Chief Musician. Set to “The Death of the Son.” A Psalm by David. I will give thanks to Yahweh with my whole heart. I will tell of all your marvelous works.
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
I will be glad and rejoice in you. I will sing praise to your name, O Most High.
3 Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
When my enemies turn back, they stumble and perish in your presence.
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
For you have maintained my just cause. You sit on the throne judging righteously.
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
You have rebuked the nations. You have destroyed the wicked. You have blotted out their name forever and ever.
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
The enemy is overtaken by endless ruin. The very memory of the cities which you have overthrown has perished.
7 Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
But Yahweh reigns forever. He has prepared his throne for judgment.
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
He will judge the world in righteousness. He will administer judgment to the peoples in uprightness.
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
Yahweh will also be a high tower for the oppressed; a high tower in times of trouble.
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
Those who know your name will put their trust in you, for you, Yahweh, have not forsaken those who seek you.
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
Sing praises to Yahweh, who dwells in Zion, and declare among the people what he has done.
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
For he who avenges blood remembers them. He doesn’t forget the cry of the afflicted.
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
Have mercy on me, Yahweh. See my affliction by those who hate me, and lift me up from the gates of death,
14 kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
that I may show all of your praise. I will rejoice in your salvation in the gates of the daughter of Zion.
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
The nations have sunk down in the pit that they made. In the net which they hid, their own foot is taken.
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
Yahweh has made himself known. He has executed judgment. The wicked is snared by the work of his own hands. (Meditation, Selah)
17 Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
The wicked shall be turned back to Sheol, even all the nations that forget God. (Sheol h7585)
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
For the needy shall not always be forgotten, nor the hope of the poor perish forever.
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
Arise, Yahweh! Don’t let man prevail. Let the nations be judged in your sight.
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)
Put them in fear, Yahweh. Let the nations know that they are only men. (Selah)

< Masalimo 9 >