< Masalimo 9 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
To the choirmaster alumoth labben a psalm of David. I will give thanks to Yahweh with all heart my I will recount all wonders your.
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
I will rejoice and I will exult in you I will sing praises to name your O Most High.
3 Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
When turn enemies my backwards they stumble and they may perish from before you.
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
For you have done justice my and cause my you have sat to a throne judging righteousness.
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
You have rebuked nations you have destroyed [the] wicked name their you have wiped out for ever and ever.
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
The enemy - they have come to an end ruins to perpetuity and cities you have plucked up it has perished memory their they.
7 Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
And Yahweh for ever he remains he has established for judgment throne his.
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
And he he will judge [the] world with righteousness he will judge [the] nations with uprightness.
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
And he may be Yahweh a refuge for the oppressed a refuge to times of trouble.
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
So they may trust in you [those who] know name your for not you have forsaken [those who] seek you O Yahweh.
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
Sing praises to Yahweh [who] dwells Zion declare among the peoples deeds his.
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
For [one who] seeks blood them he has remembered not he has forgotten [the] cry of distress of (humble [people]. *Q(K)*)
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
Show favor to me O Yahweh see affliction my from [those who] hate me O [one who] raises me from [the] gates of death.
14 kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
So that I may recount all praises your in [the] gates of [the] daughter of Zion I will rejoice in deliverance your.
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
They have sunk nations in [the] pit [which] they made in [the] net which they had hidden it has been caught foot their.
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
He has made himself known - Yahweh justice he has done by [the] work of hands his [he is] striking down [the] wicked Higgaion (Selah)
17 Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
They will return wicked [people] to Sheol all [the] nations forgetful of God. (Sheol h7585)
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
For not to perpetuity he will be forgotten [the] needy [the] hope of (afflicted [people] *Q(K)*) it will be lost for ever.
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
Arise! O Yahweh may not it prevail humankind let them be judged [the] nations on presence your.
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)
Appoint! O Yahweh - terror for them may they know [the] nations [are] human being[s] they (Selah)

< Masalimo 9 >