< Masalimo 9 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
I will praise you, O LORD, with my whole heart; I will show forth all your marvellous works.
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
I will be glad and rejoice in you: I will sing praise to your name, O you most High.
3 Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
When mine enemies are turned back, they shall fall and perish at your presence.
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
For you have maintained my right and my cause; you sat in the throne judging right.
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
You have rebuked the heathen, you have destroyed the wicked, you have put out their name for ever and ever.
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
O you enemy, destructions are come to a perpetual end: and you have destroyed cities; their memorial is perished with them.
7 Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
But the LORD shall endure for ever: he has prepared his throne for judgment.
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
And he shall judge the world in righteousness, he shall minister judgment to the people in uprightness.
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
The LORD also will be a refuge for the oppressed, a refuge in times of trouble.
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
And they that know your name will put their trust in you: for you, LORD, have not forsaken them that seek you.
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
Sing praises to the LORD, which dwells in Zion: declare among the people his doings.
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
When he makes inquisition for blood, he remembers them: he forgets not the cry of the humble.
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
Have mercy upon me, O LORD; consider my trouble which I suffer of them that hate me, you that lift me up from the gates of death:
14 kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
That I may show forth all your praise in the gates of the daughter of Zion: I will rejoice in your salvation.
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
The heathen are sunk down in the pit that they made: in the net which they hid is their own foot taken.
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
The LORD is known by the judgment which he executes: the wicked is snared in the work of his own hands. (Higgaion, Selah)
17 Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
The wicked shall be turned into hell, and all the nations that forget God. (Sheol h7585)
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
For the needy shall not always be forgotten: the expectation of the poor shall not perish for ever.
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
Arise, O LORD; let not man prevail: let the heathen be judged in your sight.
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)
Put them in fear, O LORD: that the nations may know themselves to be but men. (Selah)

< Masalimo 9 >