< Masalimo 9 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
To the chief music-maker on Muthlabben. A Psalm. Of David. I will give you praise, O Lord, with all my heart; I will make clear all the wonder of your works.
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
I will be glad and have delight in you: I will make a song of praise to your name, O Most High.
3 Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
When my haters are turned back, they will be broken and overcome before you.
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
For you gave approval to my right and my cause; you were seated in your high place judging in righteousness.
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
You have said sharp words to the nations, you have sent destruction on the sinners, you have put an end to their name for ever and ever.
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
You have given their towns to destruction; the memory of them has gone; they have become waste for ever.
7 Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
But the Lord is King for ever: he has made ready his high seat for judging.
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
And he will be the judge of the world in righteousness, giving true decisions for the peoples.
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
The Lord will be a high tower for those who are crushed down, a high tower in times of trouble;
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
And those who have knowledge of your name will put their faith in you; because you, Lord, have ever given your help to those who were waiting for you.
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
Make songs of praise to the Lord, whose house is in Zion: make his doings clear to the people.
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
When he makes search for blood, he has them in his memory: he is not without thought for the cry of the poor.
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
Have mercy on me, O Lord, and see how I am troubled by my haters; let me be lifted up from the doors of death;
14 kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
So that I may make clear all your praise in the house of the daughter of Zion: I will be glad because of your salvation.
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
The nations have gone down into the hole which they made: in their secret net is their foot taken.
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
The Lord has given knowledge of himself through his judging: the evil-doer is taken in the net which his hands had made. (Higgaion, Selah)
17 Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
The sinners and all the nations who have no memory of God will be turned into the underworld. (Sheol h7585)
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
For the poor will not be without help; the hopes of those in need will not be crushed for ever.
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
Up! O Lord; let not man overcome you: let the nations be judged before you.
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)
Put them in fear, O Lord, so that the nations may see that they are only men. (Selah)

< Masalimo 9 >