< Masalimo 9 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
【天主除暴安良】 達味詩歌,交與樂官。調寄「木特拉本」。 上主,我全心讚頌你,宣揚你的一切奇偉;
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
我要因你而歡欣踴躍,歌頌你至高者的名號。
3 Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
因為我的仇敵已經退藏,在你面前已顛仆滅亡。
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
你登上寶座,秉行公義,為我審斷了是非曲直。
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
你摧毀了異民,殲滅惡徒,你把他們的名字永遠消除。
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
敵人現已覆滅,永遠沉淪,你蕩平的城邑,全不留名。
7 Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
上主為王於永遠,安置寶座秉公審判。
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
以公義審訊世人,將以正直判決萬民。
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
上主將是受迫害者的碉堡,作他困厄中的避難所。
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
凡認識你名號的人,必仰望你,上主,尋覓你的人,你必不擯棄。
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
你們該歌頌上主,祂住在熙雍,在萬民中宣揚祂的一切化工:
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
上主追討血債,常懷念悲苦的人民,上主絕不會忘掉他慘痛的呼聲。
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
上主,求你憐憫我,垂視我仇加於我的苦辱,拯救我脫離死亡的門戶,
14 kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
好使我在熙雍女子門口,宣揚你的美譽,欣享你的助祐。
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
異民都落於自己挖掘的深坑,他們的腳都掉入自設的陷阱。
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
上主自顯於世,行了審判,惡人被自設的羅網所陷。
17 Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
願一般忘卻天主的異族,願一般惡人都歸於陰府! (Sheol h7585)
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
困苦的人絕不會被遺忘,窮人的依靠永不會喪亡。
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
上主,起來,莫讓世人獲勝,願異民盡都在你前受審!
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)
上主,懇請你恐嚇異民,使他們自知不過是人

< Masalimo 9 >