< Masalimo 89 >

1 Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara. Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya; ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.
Nitimba sifa za matendo ya uaminifu wa agano milele. Nitatangaza kweli yako kwa vizazi vijavyo.
2 Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya, kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.
Maana nimesema, “Uaminifu wa agano umeimarishwa milele; na kweli yako umeiimarisha mbinguni.”
3 Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga, ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,
“Nimefanya agano na wateule wangu, nimeapa kiapo kwa Daudi mtumishi wangu.
4 ‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya. Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’” (Sela)
Nitauimarisha uzao wako milele, na nitauimarisha utawala wako vizazi vyote.” (Selah)
5 Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova, kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.
Mbingu husifu maajabu yako, Yahwe; kweli yako inasifiwa katika kusanyiko la watakatifu.
6 Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova? Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?
Maana ni nani katika mbingu aweza kulinganishwa na Yahwe? Ambaye kati ya wana wa miungu ni kama Yahwe?
7 Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri; Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.
Ni Mungu anaye heshimiwa sana katika baraza la watakatifu naye ni wakutisha kati ya wote wanao mzunguka.
8 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu? Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.
Yahwe, Mungu wa majeshi, ni nani aliye na nguvu kama wewe, Yahwe? Kweli yako inakuzunguka.
9 Mumalamula nyanja ya mafunde awukali; pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.
Wewe huitawala bahari yenye nguvu; mawimbi yainukapo, wewe huyatuliza.
10 Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa; ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.
Ulimwangamiza Rahabu kama mmoja aliye uliwa. Uliwatawanya adui zako kwa mkono wako wenye nguvu.
11 Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu; munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.
Mbingu ni zako wewe, na nchi pia. Uliiumba dunia na vyote vilivyomo.
12 Munalenga Kumpoto ndi Kummwera; Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.
Uliumba kaskazini na kusini. Tabori na Hermoni hulifurahia jina lako.
13 Mkono wanu ndi wamphamvu; dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.
una mkono wa uweza na mkono wenye nguvu, na mkono wako wa kuume uko juu.
14 Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu; chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.
Haki na hukumu ni msingi wa kiti chako. Uaminifu wa agano lako na uaminifu huja mbele zako.
15 Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu, amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.
Wamebarikiwa watu wakuabuduo wewe! Yahwe, wanatembea katika nuru ya uso wako.
16 Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu; amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.
Siku zote wanafurahia katika jina lako, na katika haki yako wanakutukuza wewe.
17 Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.
Wewe ni fahari ya nguvu zao, na kwa nguvu zako tu washindi.
18 Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova, Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.
Maana ngao zetu ni za kwako Yahwe; mfalme wetu ni wa Mtakatifu wa Israeli.
19 Kale munayankhula mʼmasomphenya, kwa anthu anu okhulupirika munati, “Ndapatsa mphamvu wankhondo; ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.
Muda mrefu uliopita ulizungumza na waaminfu wako katika maono; ulisema, “Nimeweka taji juu ya mwenye nguvu; nimemuinua aliyechaguliwa kutoka kati ya watu.
20 Ndamupeza mtumiki wanga Davide; ndamudzoza ndi mafuta opatulika.
Nimemchagua Daudi mtumishi wangu; kwa mafuta yangu matakatifu nimempaka yeye.
21 Dzanja langa lidzamuchirikiza; zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.
Mkono wangu utamsaidia yeye; mkono wangu utamtia nguvu.
22 Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho; anthu oyipa sadzamusautsa.
Hakuna adui atakaye mdanganya; hakuna mwana wa uovu atakaye muonea.
23 Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake ndi kukantha otsutsana naye.
Nitawaangamiza adui zake mbele yake; nitawaua wale wamchukiao.
24 Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye, ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.
Kweli yangu na uaminifu wa agano vitakuwa pamoja naye; kupitia jina langu atakuwa mshindi.
25 Ndidzayika dzanja lake pa nyanja, dzanja lake lamanja pa mitsinje.
Nitaweka mkono wake juu ya bahari na mkono wake wa kuume juu ya mito.
26 Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga, Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’
Yeye ataniita, 'Wewe ni Baba yangu, Mungu wangu, na mwamba wa wokovu wangu.'
27 Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa; wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.
Nitamjalia kuwa kama mzaliwa wangu wa kwanza, aliye inuliwa zaidi juu ya wafalme wa nchi.
28 Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya, ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.
Nitaongeza uaminifu wa agano langu kwake milele; na agano langu pamoja naye litakuwa salama.
29 Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya, mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.
Nitaufanya uzao wake kudumu milele na kiti chake cha enzi kitadumu kama mbingu zilizo juu.
30 “Ngati ana ake adzataya lamulo langa ndi kusatsatira malangizo anga,
Ikiwa watoto wake wataziacha sheria zangu na kutokutii amri zangu,
31 ngati adzaswa malamulo anga ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,
na kama watazivunja sheria zangu na kutokuzishika amri zangu,
32 Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo, mphulupulu zawo powakwapula.
ndipo nitauadhiu uasi wao kwa fimbo na uovu wao kwa makofi.
33 Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye, kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.
Lakini sitauondoa kwake upendo wangu thabiti wala kutokuwa mwaminifu kwa ahadi yangu.
34 Sindidzaswa pangano langa kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.
Sitavunja agano langu wala kubadilisha maneno ya midomoni mwangu.
35 Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga ndipo sindidzanama kwa Davide,
Mara moja na kwa yote, nimeapa kwa utakatifu wangu sitamdanganya Daudi:
36 kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;
uzao wake utaendelea milele na kiti chake cha enzi kama vile jua mbele yangu.
37 udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi, mboni yokhulupirika mʼmitambo. (Sela)
Kitaimarishwa milele kama mwezi, shahidi mwaminifu mawinguni.” (Selah)
38 “Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya, mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.
Lakini wewe umemtupa na kumkataa; umemkasirikia mfalme mpakwa mafuta wako.
39 Mwakana pangano ndi mtumiki wanu ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.
Wewe umelikataa agano la mtumishi wako. Umeinajisi taji yake ardhini.
40 Inu mwagumula makoma ake onse ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.
Umevunja kuta zake zote. Umeharibu ngome yake.
41 Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake; iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.
Wapita njia wote wamemuibia, amekuwa kitu chenye kinyaa kwa majirani zake.
42 Mwakweza dzanja lamanja la adani ake; mwachititsa kuti adani ake akondwere.
Umeinua mkono wa kuume wa adui zake; umewafurahisha adui zake wote.
43 Mwabunthitsa lupanga lake, simunamuthandize pa nkhondo.
Umeyageuza makali ya upanga wake. Na hukumfanya asimame awapo vitani.
44 Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.
Umeimaliza fahari yake; umekitupa ardhini kiti chake cha enzi.
45 Mwachepetsa masiku a unyamata wake; mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi. (Sela)
Umefupisha siku za ujana wake. Umemfunika kwa aibu. (Selah)
46 “Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale? Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?
Mpaka lini, Yahwe? utajificha, milele? Mpaka lini hasira yako itawaka kama moto?
47 Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa pakuti munalenga kwachabe anthu onse!
Oh, fikiria jinsi muda wangu ulivyo mfupi, na ni kwa ajili gani umewaumba wana wote wa wanadamu wasio na manufaa!
48 Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa? Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda? (Sela) (Sheol h7585)
Ni nani aweza kuishi na asife, au atakaye iokoa nafsi yake dhidi ya mkono wa kuzimu? (Selah) (Sheol h7585)
49 Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija, chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?
Bwana, yako wapi matendo yako ya zamani ya uaminifu wa agano ambayo ulimwapia Daudi katika kweli yako?
50 Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera, momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,
Kumbuka, Bwana, watumishi wako walivyodhihakiwa na vile nilivyo vumilia moyoni mwangu matusi mengi dhidi ya mataifa.
51 mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova, ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.
Maadui zako wanavurumiza matusi, Yahwe; wanadhihaki nyayo za mpakwa mafuta wako.
52 “Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”
Atukuzwe Yahwe milele. Amina na Amina. Kitabu cha Nne

< Masalimo 89 >