< Masalimo 88 >
1 Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
わがすくひの神ヱホバよわれ晝も夜もなんぢの前にさけべり
2 Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
願くはわが祈をみまへにいたらせ汝のみみをわが號呼のこゑにかたぶけたまへ
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol )
わがたましひは患難にてみち我がいのちは陰府にちかづけり (Sheol )
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
われは穴にいるものとともにかぞへられ依仗なき人のごとくなれり
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
われ墓のうちなる殺されしもののごとく死者のうちにすてらる汝かれらを再びこころに記たまはず かれらは御手より斷滅されしものなり
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
なんぢ我をいとふかき穴 くらき處 ふかき淵におきたまひき
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
なんぢの怒はいたくわれにせまれり なんぢそのもろもろの浪をもて我をくるしめ給へり (セラ)
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
わが相識ものを我よりとほざけ我をかれらに憎ませたまへり われは錮閉されていづることあたはず
9 maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
わが眼はなやみの故をもておとろへぬ われ日ごとに汝をよべり ヱホバよなんぢに向ひてわが兩手をのべたり
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
なんぢ死者にくすしき事跡をあらはしたまはんや 亡にしもの立てなんぢを讃たたへんや (セラ)
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
汝のいつくしみは墓のうちに汝のまことは滅亡のなかに宣傳へられんや
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
汝のくすしきみわざは幽暗になんぢの義は忘失のくにに知るることあらんや
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
されどヱホバよ我なんぢに向ひてさけべり わがいのりは朝にみまへに達らん
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
ヱホバよなんぢ何なればわが霊魂をすてたまふや何なればわれに面をかくしたまふや
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
われ幼稚よりなやみて死るばかりなり我なんぢの恐嚇にあひてくるしみまどへり
16 Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
汝のはげしき怒わがうへをすぐ汝のおびやかし我をほろぼせり
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
これらの事ひねもす大水のごとく我をめぐり ことごとく來りて我をかこみふさげり
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
なんぢ我をいつくしむ者とわが友とをとほざけ わが相識るものを幽暗にいれたまへり