< Masalimo 88 >

1 Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
Yahweh God, you who rescues me, all during each day I call out [to you] to help me, and I cry out to you during each night also.
2 Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
Listen [IDM] to my prayer [DOU], while I cry out to you [for help]!
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
I have experienced many troubles/difficulties, and I am about to die [MTY] and go where dead people are. (Sheol h7585)
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
Because I have no more strength, [other people also] consider that I will soon die.
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
I am like a corpse that has been abandoned; I am like dead people who lie in their graves, people who have been completely forgotten, because you do not take care of them any more.
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
[It is as though] you have thrown me into a deep, dark pit, into a place where they throw corpses.
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
[It seems like] you are very angry with me, and [it is as though] you have crushed me like [ocean] waves [crash down on people] [MET].
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
You have caused my friends to (avoid/stay away from) me; I have become repulsive to them. [It is as though] I am in a prison and cannot escape.
9 maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
My eyes cannot see well because I cry very much. Yahweh, every day I call out to you [to help me]; I lift up my hands to you [while I pray].
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
You certainly do not [RHQ] perform miracles for dead people! Their spirits do not [RHQ] arise to praise you!
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
Corpses in the grave certainly do not tell about your faithfully loving us [RHQ], and in the place where people are finally destroyed, no one tells about what you faithfully [do for us] [RHQ].
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
No one in the deep dark pit ever sees the miracles that you perform [RHQ], and no one in the place where people have been completely forgotten tells about your being good to us.
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
But [as for me], Yahweh, I cry out to you [to help me]; each morning I pray to you.
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
Yahweh, why do you reject me [RHQ]? Why do you turn away from me [RHQ]?
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
All the time since I was young, I have suffered and have often almost died; I am (in despair/very discouraged) because of enduring the terrible things that you have done to me.
16 Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
[I feel that] you have crushed me because of your being angry with me; the terrible things that you are doing to me are almost destroying me.
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
[I feel as though] they surround me like a flood [SIM]; they are (closing in on/crushing) me from all sides.
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
You have caused [even] my friends and others whom I love to avoid me, and [it is as though] the only friend that I have is darkness.

< Masalimo 88 >