< Masalimo 88 >

1 Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
song melody to/for son: descendant/people Korah to/for to conduct upon Mahalath to/for to sing Maskil to/for Heman [the] Ezrahite LORD God salvation my day to cry in/on/with night before you
2 Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
to come (in): come to/for face: before your prayer my to stretch ear your to/for cry my
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
for to satisfy in/on/with distress: harm soul my and life my to/for hell: Sheol to touch (Sheol h7585)
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
to devise: count with to go down pit to be like/as great man nothing strength
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
in/on/with to die free like slain: killed to lie down: be dead grave which not to remember them still and they(masc.) from hand your to cut
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
to set: put me in/on/with pit lower in/on/with darkness in/on/with depth
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
upon me to support rage your and all wave your to afflict (Selah)
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
to remove to know my from me to set: make me abomination to/for them to restrain and not to come out: come
9 maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
eye my to languish from affliction to call: call to you LORD in/on/with all day to spread to(wards) you palm my
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
to/for to die to make: do wonder if: surely no shade to arise: rise to give thanks you (Selah)
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
to recount in/on/with grave kindness your faithfulness your in/on/with Abaddon
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
to know in/on/with darkness wonder your and righteousness your in/on/with land: country/planet forgetfulness
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
and I to(wards) you LORD to cry and in/on/with morning prayer my to meet you
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
to/for what? LORD to reject soul my to hide face your from me
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
afflicted I and to die from youth to lift: bear terror your to distract
16 Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
upon me to pass burning anger your terror your to destroy me
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
to turn: surround me like/as water all [the] day to surround upon me unitedness
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
to remove from me to love: lover and neighbor to know my darkness

< Masalimo 88 >