< Masalimo 88 >

1 Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
[A Song. A Psalm by the sons of Korah. For the Chief Musician. To the tune of "The Suffering of Affliction." A contemplation by Heman, the Ezrahite.] LORD, the God of my salvation, I have cried day and night before you.
2 Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
Let my prayer enter into your presence. Turn your ear to my cry.
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
For my soul is full of troubles. My life draws near to Sheol. (Sheol h7585)
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
I am counted among those who go down into the pit. I am like a man who has no help,
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
set apart among the dead, like the slain who lie in the grave, whom you remember no more. They are cut off from your hand.
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
You have laid me in the lowest pit, in the darkest depths.
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
Your wrath lies heavily on me. You have afflicted me with all your waves. (Selah)
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
You have taken my friends from me. You have made me an abomination to them. I am confined, and I can't escape.
9 maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
My eyes are dim from grief. I have called on you daily, LORD. I have spread out my hands to you.
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
Do you show wonders to the dead? Do the dead rise up and praise you? (Selah)
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
Is your loving kindness declared in the grave? Or your faithfulness in Destruction?
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
Are your wonders made known in the dark? Or your righteousness in the land of forgetfulness?
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
But to you, LORD, I have cried. In the morning, my prayer comes before you.
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
LORD, why do you reject my soul? Why do you hide your face from me?
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
I am afflicted and ready to die from my youth up. While I suffer your terrors, I am distracted.
16 Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
Your fierce wrath has gone over me. Your terrors have cut me off.
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
They came around me like water all day long. They completely engulfed me.
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
You have put lover and friend far from me, and my friends into darkness.

< Masalimo 88 >