< Masalimo 88 >

1 Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
A Song, a Psalm for the sons of Korah. To the chief Musician. Upon Mahalath Leannoth. An instruction. Of Heman the Ezrahite. Jehovah, God of my salvation, I have cried by day [and] in the night before thee.
2 Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
Let my prayer come before thee; incline thine ear unto my cry.
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
For my soul is full of troubles, and my life draweth nigh to Sheol. (Sheol h7585)
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
I am reckoned with them that go down into the pit; I am as a man that hath no strength:
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
Prostrate among the dead, like the slain that lie in the grave; whom thou rememberest no more, and who are cut off from thy hand.
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
Thou hast laid me in the lowest pit, in dark places, in the deeps.
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
Thy fury lieth hard upon me, and thou hast afflicted [me] with all thy waves. (Selah)
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
Thou hast put my familiar friends far from me; thou hast made me an abomination unto them: I am shut up, and I cannot come forth.
9 maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
Mine eye consumeth by reason of affliction. Upon thee, Jehovah, have I called every day; I have stretched out my hands unto thee.
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
Wilt thou do wonders to the dead? shall the shades arise and praise thee? (Selah)
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
Shall thy loving-kindness be declared in the grave? thy faithfulness in Destruction?
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
Shall thy wonders be known in the dark? and thy righteousness in the land of forgetfulness?
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
But as for me, Jehovah, I cry unto thee, and in the morning my prayer cometh before thee.
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
Why, O Jehovah, castest thou off my soul? [why] hidest thou thy face from me?
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
I am afflicted and expiring from my youth up; I suffer thy terrors, [and] I am distracted.
16 Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
Thy fierce anger hath gone over me; thy terrors have brought me to nought:
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
They have surrounded me all the day like water; they have compassed me about together.
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
Lover and associate hast thou put far from me: my familiar friends are darkness.

< Masalimo 88 >