< Masalimo 88 >

1 Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
A Canticle Psalm to the sons of Korah. Unto the end. For Mahalath, to answer the understanding of Heman the Ezrahite. O Lord, God of my salvation: I have cried out, day and night, in your presence.
2 Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
Let my prayer enter in your sight. Incline your ear to my petition.
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
For my soul has been filled with evils, and my life has drawn near to Hell. (Sheol h7585)
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
I am considered to be among those who will descend into the pit. I have become like a man without assistance,
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
idle among the dead. I am like the wounded sleeping in sepulchers, whom you no longer remember, and who have been repelled by your hand.
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
They have lain me in the lower pit: in dark places and in the shadow of death.
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
Your fury has been confirmed over me. And you have brought all your waves upon me.
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
You have sent my acquaintances far from me. They have set me as an abomination to themselves. I was handed over, yet I did not depart.
9 maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
My eyes languished before destitution. All day long, I cried out to you, O Lord. I stretched out my hands to you.
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
Will you perform wonders for the dead? Or will physicians raise to life, and so confess to you?
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
Could anyone declare your mercy in the sepulcher, or your truth from within perdition?
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
Will your wonders be known in the darkness, or your justice in the land of oblivion?
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
And I have cried out to you, O Lord, and in early morning, my prayer will come before you.
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
Lord, why do you reject my prayer? Why do you turn your face away from me?
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
I am poor, and I have been amid hardships from my youth. And, though I have been exalted, I am humbled and disturbed.
16 Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
Your wrath has crossed into me, and your terrors have disturbed me.
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
They have surrounded me like water, all day long. They have surrounded me, all at once.
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
Friend and neighbor, and my acquaintances, you have sent far away from me, away from misery.

< Masalimo 88 >