< Masalimo 88 >

1 Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
A song. A Psalm of the sons of Korah. For the choirmaster. According to Mahalath Leannoth. A Maskil of Heman the Ezrahite. O LORD, the God of my salvation, day and night I cry out before You.
2 Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
May my prayer come before You; incline Your ear to my cry.
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
For my soul is full of troubles, and my life draws near to Sheol. (Sheol h7585)
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
I am counted among those descending to the Pit. I am like a man without strength.
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
I am forsaken among the dead, like the slain who lie in the grave, whom You remember no more, who are cut off from Your care.
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
You have laid me in the lowest Pit, in the darkest of the depths.
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
Your wrath weighs heavily upon me; all Your waves have submerged me.
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
You have removed my friends from me; You have made me repulsive to them; I am confined and cannot escape.
9 maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
My eyes grow dim with grief. I call to You daily, O LORD; I spread out my hands to You.
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
Do You work wonders for the dead? Do departed spirits rise up to praise You?
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
Can Your loving devotion be proclaimed in the grave, Your faithfulness in Abaddon?
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
Will Your wonders be known in the darkness, or Your righteousness in the land of oblivion?
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
But to You, O LORD, I cry for help; in the morning my prayer comes before You.
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
Why, O LORD, do You reject me? Why do You hide Your face from me?
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
From my youth I was afflicted and near death. I have borne Your terrors; I am in despair.
16 Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
Your wrath has swept over me; Your terrors have destroyed me.
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
All day long they engulf me like water; they enclose me on every side.
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
You have removed my beloved and my friend; darkness is my closest companion.

< Masalimo 88 >