< Masalimo 88 >
1 Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
Wer. Zaburi mar yawuot Kora. Kuom jatend wer. Kaluwore gi mahalath leanoth. Maskil mar Heman ja-Ezra. Yaye Jehova Nyasaye, in e Nyasacha ma resa, aywagora e nyimi odiechiengʼ gotieno.
2 Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
Mad lamona chop e nyimi; yie ilok iti ne kwayona.
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol )
Nimar chandruok opongʼo chunya kendo ngimana sudo machiegni gi liel. (Sheol )
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
Ikwana kaachiel gi joma ridore piny ei bur matut; achalo ngʼama onge teko.
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
Ojwangʼa kaachiel gi joma otho, mana kaka joma onegi monindo e bur, makoro ok ipar kuomgi kendo, joma ongʼad kargi oko e ritni.
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
Iseketa ei bur matut mogik, ei piny mogik, kama olil ti.
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
Mirimbi mager ogore kuoma mapek; isetamo wangʼa gi apaka magi duto. (Sela)
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
Isemiyo osiepena mane ni machiegni koda mogik oringa, kendo isemiyo koro achalonegi mana koko. Odinna ma ok anyal tony;
9 maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
wengena ok nen maber nikech kuyo ma an-go. Aluongi odiechiengʼ kodiechiengʼ, yaye Jehova Nyasaye; achikoni lwetena.
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
Bende itimo honni magi ne joma otho? Joma otho bende nyalo chier kendo mi paki? (Sela)
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
Herani bende inyiso joma ni ei liel; adier, koso adierani bende yudore e kethruok piny?
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
Timbeni miwuoro bende ongʼere kama otimo mudhono, kata timbeni makare e piny ma ilalieno?
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
Anto aywakni mondo ikonya, yaye Jehova Nyasaye; lamona chopo e nyimi gokinyi.
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
Yaye Jehova Nyasaye, angʼo momiyo idaga kendo ipandona wangʼi?
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
Aseneno chandruok chakre tin-na mi adwa tho; asewinjo malit nikech thagruok misekelona, kendo chunya oseol.
16 Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
Mirimbi mager oseywaya; thagruok mimiya osetieka.
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
Gilwora ka ataro odiechiengʼ duto; gisedinona chuth koni gi koni.
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
Isemaya osiepena gi joherana; mudho mandiwa ema koro odongʼ machiegni koda kaka osiepna.