< Masalimo 88 >

1 Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
Pjesma. Psalam. Sinova Korahovih. Zborovođi. Po napjevu “Bolest”. Za pjevanje. Poučna pjesma. Ezrahijca Hemana. Jahve, Bože moj, vapijem danju, a noću naričem pred tobom.
2 Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
Neka dopre do tebe molitva moja, prigni uho k vapaju mome.
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
Jer mi je duša zasićena patnjama, moj se život bliži Podzemlju. (Sheol h7585)
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
Broje me k onima što u grob silaze, postadoh sličan nemoćniku.
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
Među mrtvima moj je ležaj, poput ubijenih što leže u grobu kojih se više ne spominješ, od kojih si ustegao ruku.
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
Smjestio si me u jamu duboku, u tmine, u bezdan.
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
Teško me pritišće ljutnja tvoja i svim me valima svojim prekrivaš.
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
Udaljio si od mene znance moje, Óučini da im gnusan budem: zatvoren sam, ne mogu izaći.
9 maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
Od nevolje oči mi gasnu: vapijem tebi, Jahve, iz dana u dan, za tobom ruke pružam.
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
Zar na mrtvima činiš čudesa? Zar će sjene ustati i hvaliti tebe?
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
Zar se u grobu pripovijeda o tvojoj dobroti? O vjernosti tvojoj u Propasti?
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
Zar se u tmini objavljuju čudesa tvoja i tvoja pravda u Zaboravu?
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
Ipak ja vapijem tebi, Jahve, prije jutra molitvom te pretječem.
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
Zašto, Jahve, odbacuješ dušu moju? Zašto sakrivaš lice od mene?
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
Bijedan sam i umirem već od dječaštva, klonuh noseći tvoje strahote.
16 Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
Preko mene prijeđoše vihori tvojega gnjeva, strahote me tvoje shrvaše,
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
okružuju me kao voda sveudilj, optječu me svi zajedno.
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
Udaljio si od mene prijatelja i druga: mrak mi je znanac jedini.

< Masalimo 88 >