< Masalimo 88 >

1 Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
詠【哀怨歌】 科辣黑子孫的詩歌,交於樂官,悲調歌唱。 上主,我的天主,我白天禱告,我黑夜在您的面前哀號。
2 Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
願我的祈禱上前達您前,求您側耳聽我的呼喊。
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
因我的心靈飽受災難,我的性命已臨近陰間; (Sheol h7585)
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
我已被列在進入墳墓的人中,我已變成與無氣力的人相同。
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
我的床榻舖在死人的中間,與葬於墳墓者的屍身作伴,您已不再記念他們,您已不再照顧他們。
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
您把我放在極深的坑間,您把我置於黑暗和深淵。
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
您的忿怒氣燄重壓著我,您的大浪巨濤苦害著我。
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
您叫我的知己離我遠去,您使我被他們痛恨厭惡;我受他們拘留不得外出。
9 maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
我的眼睛痛苦而憔悴,上主,我天天在呼號著您,也把我的雙手向您舉起。
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
難道您還要給死人發顯奇跡,或是去世的人會起來稱謝您?
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
難道在墳墓裏還有人稱述您的仁慈,或者在陰府內還有人宣揚您的信義?
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
難道在幽暗處能有人明瞭您的奇蹟?或者在遺忘區還有人曉得您的正義?
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
但是上主,我現今呼號您,我的祈禱早晨上達於您;
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
上主,您為什麼捨棄了我的靈魂?又為什麼向我掩起了您的慈容?
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
我自幼受苦,幾乎死去,受您的威嚇,萬分恐懼;
16 Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
您的盛怒將我淹沒,您的威嚇使我死掉,
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
像水一樣常環繞著我,由四周齊來緊圍著我。
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
您使親友同伴將我離棄,黑暗成了我的家人知己。

< Masalimo 88 >