< Masalimo 87 >

1 Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
Синів Коре́євих. Псалом, Пісня.
2 Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
Госпо́дь любить брами Сіону понад усі се́лища Яковові.
3 Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
Славне розповіда́ють про тебе, місто Боже! (Се́ла)
4 “Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
„Тим, хто знає мене, нагадаю про Ра́гав та про Вавило́н; ось Филисте́я та Тир з Ку́шем кажуть: Отой народився був там“.
5 Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
І про Сіон говори́тимуть: „Той і той народився був у ньому, й Сам Всевишній зміцняє його́“!
6 Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
Господь буде лічити у книзі наро́дів: „Оцей народився був там“! (Се́ла)
7 Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”
І співають, і грають вони: „У Тобі — всі джере́ла мої!“

< Masalimo 87 >