< Masalimo 87 >
1 Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
En Psalmvisa Korah barnas. Han är fast grundad på de helga bergen.
2 Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
Herren älskar Zions portar, öfver alla Jacobs boningar.
3 Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
Härlig ting varda i dig predikade, du Guds stad. (Sela)
4 “Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
Jag vill predika låta för Rahab och Babel, att de mig känna skola. Si, de Philisteer och Tyrer, samt med de Ethioper, varda der födde.
5 Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
Man skall i Zion säga, att allahanda folk derinne födt varder, och att han, den Högste, bygger honom.
6 Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
Herren skall predika låta i allahanda tungomål, att ock någre af dem skola der födde varda. (Sela)
7 Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”
Och de sångare skola alle i dig sjunga till skiftes, såsom i en dans.