< Masalimo 87 >
1 Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
Un psaume par les fils de Korah; un chant. Son fondement est dans les montagnes saintes.
2 Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
Yahvé aime les portes de Sion plus que toutes les habitations de Jacob.
3 Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
On dit de toi des choses glorieuses, cité de Dieu. (Selah)
4 “Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
J'inscrirai Rahab et Babylone parmi ceux qui me reconnaissent. Voici la Philistie, Tyr, et aussi l'Éthiopie: « Celui-ci est né là-bas. »
5 Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
Oui, on dira de Sion: « Untel et untel sont nés en elle ». le Très-Haut lui-même l'établira.
6 Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
L'Éternel fera le compte, quand il écrira les peuples, « Celui-ci est né là. (Selah)
7 Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”
Ceux qui chantent comme ceux qui dansent disent, « Tous mes ressorts sont en toi. »