< Masalimo 87 >
1 Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
A PSALM OF THE SONS OF KORAH. A SONG. His foundation [is] in holy mountains.
2 Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
YHWH is loving the gates of Zion Above all the dwelling places of Jacob.
3 Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
Honorable things are spoken in You, O city of God. (Selah)
4 “Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
I mention Rahab and Babel to those knowing Me, Behold, Philistia, and Tyre, with Cush! This [one] was born there.
5 Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
And of Zion it is said: Each one was born in her, And He, the Most High, establishes her.
6 Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
YHWH recounts in the describing of the peoples, “This [one] was born there.” (Selah)
7 Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”
Also singers as players on instruments, All my fountains [are] in You!