< Masalimo 87 >

1 Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
Han har grundlagt en Stad paa de hellige Bjerge.
2 Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
Herren elsker Zions Porte fremfor alle Jakobs Boliger.
3 Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
Der er herlige Ting sagt i dig, du Guds Stad! (Sela)
4 “Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
Jeg vil nævne Rahab og Babel iblandt dem, som kende mig; se, Filisteren og Tyrieren samt Morianen: „Denne, han er født der.‟
5 Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
Men til Zion skal der siges: Denne og hin er født i den, den Højeste selv skal befæste den.
6 Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
Herren skal tælle, naar han opskriver Folkene, og sige: „Denne er født der.‟ (Sela)
7 Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”
Og de, som synge, tillige med dem, som danse, skulle sige: Alle mine Kilder ere i dig.

< Masalimo 87 >