< Masalimo 87 >
1 Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
Synům Chóre, žalm a píseň. Základ svůj na horách svatých.
2 Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
Milujeť Hospodin, totiž brány Sionské, nade všecky příbytky Jákobovy.
3 Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
Přeslavnéť jsou to věci, kteréž se o tobě hlásají, ó město Boží. (Sélah)
4 “Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
Připomínati budu Egypt a Babylon před svými známými, ano i Filistinské a Tyrské i Mouřeníny, že se tu každý z nich narodil.
5 Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
An i o Sionu praveno bude: Ten i onen jest rodem z něho, sám pak Nejvyšší utvrdí jej.
6 Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
Sečteť Hospodin při popisu národy, a dí, že tento se tu narodil. (Sélah)
7 Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”
Tou příčinou zpívají s plésáním o tobě všecky moci života mého.