< Masalimo 86 >

1 Pemphero la Davide. Ndimvereni Yehova ndipo mundiyankhe, pakuti ndine wosauka ndi wosowa.
Umkhuleko kaDavida Zwana, Oh Thixo, ungiphendule, ngoba ngingumyanga ngiyaswela.
2 Yangʼanirani moyo wanga, pakuti ndine wodzipereka kwa Inu. Inu ndinu Mulungu wanga; pulumutsani mtumiki wanu amene amadalira Inu. Inu ndinu Mulungu wanga.
Vikela impilo yami, ngoba ngizinikele kuwe; sindisa inceku yakho ekuthembayo; UnguNkulunkulu wami.
3 Mundichitire chifundo, Inu Ambuye, pakuti ndikuyitana Inu tsiku lonse.
Woba lesihawu kimi, Oh Thixo, ngoba ngitshona ngikubiza ilanga lonke.
4 Bweretsani chimwemwe kwa mtumiki wanu, Ambuye, pakuti ndimadalira Inu.
Letha ukuthokoza encekwini yakho, ngoba kuwe, Oh Thixo, ngiphakamisela umphefumulo wami.
5 Inu Ambuye, ndinu wokhululuka ndi wabwino, wodzaza ndi chikondi kwa onse amene amayitana Inu.
Uyathethelela njalo ulungile, Oh Thixo, ugcwele uthando kulabo abakhuleka kuwe.
6 Yehova imvani pemphero langa; mvetserani kulira kwanga kofuna chifundo.
Zwana umkhuleko wami, Oh Thixo; lalela ukukhala kwami ngicela umusa.
7 Pa tsiku la mavuto anga ndidzayitana Inu, pakuti Inu mudzandiyankha.
Mhla ngiphakathi kokuhlupheka ngizakhala kuwe, ngoba uzangiphendula.
8 Pakati pa milungu palibe wina wofanana nanu Ambuye; palibe ntchito zolingana ndi ntchito zanu.
Phakathi kwabonkulunkulu kakho onjengawe, Oh Thixo; kakulazenzo ezingalinganiswa lezakho.
9 Mitundu yonse ya anthu imene munayipanga idzabwera ndi kudzalambira pamaso panu Ambuye; iwo adzabweretsa ulemerero pa dzina lanu.
Zonke izizwe owazenzayo zizakuza zikhonze kuwe, Nkosi; zizaletha udumo ebizweni lakho.
10 Pakuti ndinu wamkulu ndipo mumachita zodabwitsa; Inu nokha ndiye Mulungu.
Ngoba umkhulu njalo wenza imisebenzi emangalisayo; wena wedwa unguNkulunkulu.
11 Ndiphunzitseni njira yanu Yehova, ndipo ndidzayenda mʼchoonadi chanu; patseni mtima wosagawikana kuti ndilemekeze dzina lanu.
Ngifundisa indlela yakho, Oh Thixo, ukuze ngihambe eqinisweni lakho; ngipha inhliziyo engaxamalazanga, ukuze ngilesabe ibizo lakho.
12 Ndidzakutamandani Ambuye Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse; ndidzalemekeza dzina lanu kwamuyaya.
Ngizakudumisa, Nkosi Nkulunkulu wami, ngenhliziyo yami yonke; ngizalidumisa ibizo lakho laphakade.
13 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu kwa ine; mwandipulumutsa ku malo ozama a manda. (Sheol h7585)
Ngoba lukhulu uthando lwakho kimi; ungenyule ekujuleni kwendawo yabafileyo. (Sheol h7585)
14 Inu Mulungu wanga, anthu odzikuza akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufuna kundipha, amene salabadira za Inu.
Iziqholo ziyangihlasela, Oh Nkulunkulu iqembu lamadoda alesihluku lizingela impilo yami abantu abangakunanziyo wena.
15 Koma Ambuye ndinu Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi ndi wokhulupirika.
Kodwa wena, Nkosi, unguNkulunkulu olozwelo, olobubelo, ophuza ukuzonda, owandayo ngothando lokuthembeka.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo ndichitireni chifundo; perekani mphamvu zanu kwa mtumiki wanu ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.
Phendukela ngakimi ube lesihawu kimi; veza amandla akho ngenceku yakho, ngisindise ngoba ngiyakukhonza, njengokwenziwa ngumama.
17 Mundionetse chizindikiro cha ubwino wanu kuti adani achione ndi kuchititsidwa manyazi, pakuti Yehova mwandithandiza ndi kunditonthoza.
Ngipha isiboniso sokulunga kwakho, ukuze izitha zami zisibone ziyangeke, ngoba wena, Oh Thixo, usungisizile njalo wangiduduza.

< Masalimo 86 >