< Masalimo 86 >
1 Pemphero la Davide. Ndimvereni Yehova ndipo mundiyankhe, pakuti ndine wosauka ndi wosowa.
Libondeli ya Davidi. Yawe, yoka mpe yanola ngai; pamba te nazali mobola mpe moto akelela.
2 Yangʼanirani moyo wanga, pakuti ndine wodzipereka kwa Inu. Inu ndinu Mulungu wanga; pulumutsani mtumiki wanu amene amadalira Inu. Inu ndinu Mulungu wanga.
Batela bomoi na ngai, pamba te nazali moyengebene na Yo. Yo, Nzambe na ngai, bikisa ngai, mosali na Yo, oyo natiaka elikya kati na Yo.
3 Mundichitire chifundo, Inu Ambuye, pakuti ndikuyitana Inu tsiku lonse.
Oh Nkolo, yokela ngai mawa; pamba te nabelelaka Yo tango nyonso!
4 Bweretsani chimwemwe kwa mtumiki wanu, Ambuye, pakuti ndimadalira Inu.
Nkolo, sepelisa motema na ngai, mosali na Yo, pamba te natombolaka molimo na ngai epai na Yo.
5 Inu Ambuye, ndinu wokhululuka ndi wabwino, wodzaza ndi chikondi kwa onse amene amayitana Inu.
Nkolo, ozali malamu, olimbisaka, otonda na bolingo mpo na bato nyonso oyo babelelaka Yo.
6 Yehova imvani pemphero langa; mvetserani kulira kwanga kofuna chifundo.
Yawe, yoka losambo na ngai, yoka libondeli na ngai!
7 Pa tsiku la mavuto anga ndidzayitana Inu, pakuti Inu mudzandiyankha.
Na mokolo ya pasi na ngai, nabelelaka Yo, pamba te oyanolaka ngai.
8 Pakati pa milungu palibe wina wofanana nanu Ambuye; palibe ntchito zolingana ndi ntchito zanu.
Nkolo, nzambe moko te ekokani na Yo, kati na banzambe; moko te ekoki kosala makambo oyo Yo osalaka.
9 Mitundu yonse ya anthu imene munayipanga idzabwera ndi kudzalambira pamaso panu Ambuye; iwo adzabweretsa ulemerero pa dzina lanu.
Nkolo, bikolo nyonso oyo osala ekoya kogumbama liboso na Yo mpe ekoya kopesa Kombo na Yo nkembo.
10 Pakuti ndinu wamkulu ndipo mumachita zodabwitsa; Inu nokha ndiye Mulungu.
Pamba te ozali monene mpe osalaka bikamwa; Yo kaka nde ozali Nzambe.
11 Ndiphunzitseni njira yanu Yehova, ndipo ndidzayenda mʼchoonadi chanu; patseni mtima wosagawikana kuti ndilemekeze dzina lanu.
Yawe, lakisa ngai nzela na Yo, mpe nakotambola kolanda bosolo na Yo. Pesa ngai motema ya sembo mpo ete natosa Yo.
12 Ndidzakutamandani Ambuye Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse; ndidzalemekeza dzina lanu kwamuyaya.
Nkolo, Nzambe na ngai, nakosanzola Yo, na motema na ngai mobimba, nakopesa Kombo na Yo nkembo mpo na Yo libela.
13 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu kwa ine; mwandipulumutsa ku malo ozama a manda. (Sheol )
Pamba te bolingo na Yo mpo na ngai ezali monene, mpe okangolaki ngai wuta na mozindo ya mboka ya bakufi. (Sheol )
14 Inu Mulungu wanga, anthu odzikuza akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufuna kundipha, amene salabadira za Inu.
Nzambe, bato ya lofundu bazali kobundisa ngai, mpe ngulupa ya bato na kanza bazali koluka koboma ngai; batosaka Yo ata moke te.
15 Koma Ambuye ndinu Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi ndi wokhulupirika.
Kasi Yo Nkolo, ozali Nzambe na mawa mpe na ngolu, osilikaka noki te, otonda na bolingo mpe na boyengebene.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo ndichitireni chifundo; perekani mphamvu zanu kwa mtumiki wanu ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.
Balola elongi na Yo epai na ngai mpe yokela ngai mawa; pesa ngai, mosali na Yo, makasi mpe bikisa ngai mwana ya mwasi mosali na Yo!
17 Mundionetse chizindikiro cha ubwino wanu kuti adani achione ndi kuchititsidwa manyazi, pakuti Yehova mwandithandiza ndi kunditonthoza.
Salela ngai elembo ya boboto na Yo mpo ete banguna na ngai bamona yango mpe bakufa soni! Yawe, ozali Mosungi mpe Mobondi na ngai.