< Masalimo 86 >
1 Pemphero la Davide. Ndimvereni Yehova ndipo mundiyankhe, pakuti ndine wosauka ndi wosowa.
Lemo mar Daudi. Winj lamona, yaye Jehova Nyasaye, kendo dwoka, nimar adhier kendo achando.
2 Yangʼanirani moyo wanga, pakuti ndine wodzipereka kwa Inu. Inu ndinu Mulungu wanga; pulumutsani mtumiki wanu amene amadalira Inu. Inu ndinu Mulungu wanga.
Rit ngimana, nikech achiworani. In e Nyasacha, omiyo res ngima jatichni, mogeno kuomi.
3 Mundichitire chifundo, Inu Ambuye, pakuti ndikuyitana Inu tsiku lonse.
Kecha, yaye Ruoth Nyasaye, nimar aywakni odiechiengʼ duto.
4 Bweretsani chimwemwe kwa mtumiki wanu, Ambuye, pakuti ndimadalira Inu.
Mi jatichni obed mamor, yaye Ruoth Nyasaye, nimar in ema aketo genona kuomi.
5 Inu Ambuye, ndinu wokhululuka ndi wabwino, wodzaza ndi chikondi kwa onse amene amayitana Inu.
Nikech in iber kendo iweyo richo, yaye Ruoth Nyasaye in gihera mangʼeny kuom joma luongi.
6 Yehova imvani pemphero langa; mvetserani kulira kwanga kofuna chifundo.
Winj lamona, yaye Jehova Nyasaye; chik iti ne ywakna ma akwayigo kech.
7 Pa tsiku la mavuto anga ndidzayitana Inu, pakuti Inu mudzandiyankha.
Chiengʼ ma chandruok omaka to abiro luongi mondo ikonya, nimar ibiro dwoka.
8 Pakati pa milungu palibe wina wofanana nanu Ambuye; palibe ntchito zolingana ndi ntchito zanu.
Onge nyasaye moro amora e dier nyiseche machalo kodi, yaye Ruoth Nyasaye; onge timbe minyalo pimo gi magi.
9 Mitundu yonse ya anthu imene munayipanga idzabwera ndi kudzalambira pamaso panu Ambuye; iwo adzabweretsa ulemerero pa dzina lanu.
Ogendini duto michweyo biro lami kapodho e nyimi, yaye Ruoth Nyasaye; bende gibiro miyo nyingi duongʼ.
10 Pakuti ndinu wamkulu ndipo mumachita zodabwitsa; Inu nokha ndiye Mulungu.
Nimar iduongʼ kendo itimo timbe miwuoro; in e Nyasaye kende.
11 Ndiphunzitseni njira yanu Yehova, ndipo ndidzayenda mʼchoonadi chanu; patseni mtima wosagawikana kuti ndilemekeze dzina lanu.
Puonja yoreni, yaye Jehova Nyasaye, mondo eka awuothi e adierani; miya chuny ma ok ba koni gi koni, mondo omi aluor nyingi.
12 Ndidzakutamandani Ambuye Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse; ndidzalemekeza dzina lanu kwamuyaya.
Abiro paki gi chunya duto, yaye Ruoth Nyasacha, abiro miyo nyingi duongʼ nyaka chiengʼ.
13 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu kwa ine; mwandipulumutsa ku malo ozama a manda. (Sheol )
Nimar (hera) ma iherago duongʼ, kendo isegola ei chuny bur matut. (Sheol )
14 Inu Mulungu wanga, anthu odzikuza akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufuna kundipha, amene salabadira za Inu.
Josunga ma wengegi tek monja, yaye Nyasaye; migawo mar joma ok kech ngʼato dwaro tieko ngimana, joma ok dew kata in.
15 Koma Ambuye ndinu Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi ndi wokhulupirika.
In to in Nyasaye ma kecho kendo ngʼwon, yaye Jehova Nyasaye, iyi ok wangʼ piyo, ipongʼ gihera kendo in ja-adiera.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo ndichitireni chifundo; perekani mphamvu zanu kwa mtumiki wanu ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.
Duog ira mondo ikecha; med jatichni tekoni, kendo res jatichni mogeni.
17 Mundionetse chizindikiro cha ubwino wanu kuti adani achione ndi kuchititsidwa manyazi, pakuti Yehova mwandithandiza ndi kunditonthoza.
Miyae ranyisi mar berni, mondo wasika one mi wigi okuodi, nimar in ema isebedo ka ikonya kendo ihoya, yaye Jehova Nyasaye.