< Masalimo 85 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
Yahwe, wewe umeonesha fadhilia kwenye nchi yako; umeurejesha ustawi wa Yakobo.
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
Umesamehe dhambi ya watu wako; umezisitiri dhambi zao zote. (Selah)
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
Umeondoa ghadhabu yako yote; umeiacha hasira yako kali.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Uturejeshe sisi, Ee Mungu wa wokovu wetu, na uikomeshe chuki yako juu yetu.
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Je! Utaendelea kuwa na hasira juu yetu milele? utadumisha hasira kizazi chote kijacho?
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
Je, hautatuhuisha tena? Kisha watu wako watafurahia katika wewe.
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
Utuoneshe sisi uaminifu wa agano lako, Yahwe, utupe sisi wokovu wako.
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
Nitasikiliza yale Yahwe Mungu asemayo, maana yeye atafanya amani pamoja na watu wake, wafuasi wake waminifu. Lakini lazima wasirudi tena katika njia za kipumbavu.
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
Hakika wokovu wake u karibu na wale wanao mwabudu yeye; kisha utukufu utabaki katika nchi yetu.
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
Uaminifu wa agano na uaminifu vimekutana pamoja; haki na amani vimebusiana.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
Uaminifu unatoa chemchem kutoka ardhini, na haki hutazama chini kutoka mawinguni.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
Ndiyo, Yahwe atatoa baraka zake njema, na nchi itatoa mazao yake.
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
Haki itaenda mbele zake na kufanya njia kwa ajili ya nyayo zake.

< Masalimo 85 >