< Masalimo 85 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
Para el director del coro. Un salmo de los descendientes de Coré Señor, le has mostrado tu bondad a la tierra; has restaurado la prosperidad de Jacob.
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
Quitaste la culpa de tu pueblo; perdonaste todos sus pecados. (Selah)
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
Retiraste tu furia; y te alejaste de tu feroz ira.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Acércanos otra vez a ti, ¡Dios de nuestra salvación! Aleja tu ira de nosotros.
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
¿Vas a estar furioso con nosotros para siempre? ¿Permanecerás airado con todas nuestras generaciones futuras?
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
¿No restaurarás nuestras vidas, de tal modo que tu pueblo pueda hallar felicidad en ti?
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
¡Señor, muéstranos tu misericordioso amor! ¡Danos tu salvación!
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
Déjame escuchar la voluntad de Dios. Dios habla paz a su pueblo, a aquellos que confían en él. Pero ellos no deben volver por sus caminos necios.
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
Verdaderamente que la salvación de Dios está con los que hacen lo que él ordena. Su presencia gloriosa vivirá con nosotros en nuestra tierra.
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
El amor y la verdad se encontrarán; la bondad y la paz se besarán mutuamente.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
Lo que es verdad crecerá de la tierra; y lo que es justo se dejará ver desde los cielos.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
Dios nos dará ciertamente todo lo que es bueno, y nuestra tierra producirá finos cultivos.
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
La verdad y la justicia saldrán de él para prepararle camino y que pueda pasar.

< Masalimo 85 >