< Masalimo 85 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
Til songmeisteren; av Korahs born, ein salme. Herre, du hev vore nådig mot landet ditt, du hev gjort vending i Jakobs fangeskap.
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
Du hev teke burt ditt folks skuld, du hev breidt yver alle deira synder. (Sela)
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
Du hev teke burt all din harm, du hev vendt deg frå din brennande vreide.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Vend um til oss, vår Frelse-Gud, og gjer ende på din uvilje imot oss!
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Vil du æveleg vera vreid på oss? Vil du lata din vreide vara frå ætt til ætt?
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
Vil ikkje du gjera oss livande att, so ditt folk kann gleda seg i deg?
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
Herre, lat oss sjå di miskunn, og gjev oss di frelsa!
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
Eg vil høyra kva Gud Herren talar, for han talar fred til sitt folk og til sine trugne - berre dei ikkje vender um att til dårskap.
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
Ja, hans frelsa er nær deim som ottast honom, so herlegdom skal bu i vårt land.
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
Miskunn og truskap skal møta kvarandre, rettferd og fred kyssa kvarandre.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
Truskap skal renna upp av jordi, og rettferd skoda ned frå himmelen.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
Herren skal og gjeva det som gode, og vårt land skal gjeva si grøda.
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
Rettferd skal ganga fyre honom og gjera hans fotspor til sin veg.