< Masalimo 85 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
Pour la fin, aux fils de Coré, psaume. Vous avez béni, Seigneur, votre terre; vous avez détourné la captivité de Jacob.
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
Vous avez remis l’iniquité de votre peuple, vous avez couvert tous leurs péchés.
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
Vous avez apaisé votre colère, vous avez détourné votre peuple de la colère de votre indignation.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Convertissez-nous, ô Dieu notre Sauveur; et détournez votre colère de nous.
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Est-ce que vous serez éternellement en colère; ou étendrez-vous votre colère de génération en génération?
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
Ô Dieu, revenez à nous, vous nous donnerez la vie, et votre peuple se réjouira en vous.
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
Montrez-nous, Seigneur, votre miséricorde; et donnez-nous votre salut.
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
J’écouterai ce que dira au dedans de moi le Seigneur Dieu, parce qu’il parlera paix pour son peuple, Et pour ses saints, et pour ceux qui se tournent vers leur cœur.
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
Assurément, près de ceux qui le craignent est son salut, afin que la gloire habite dans notre terre.
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
La miséricorde et la vérité se sont rencontrées; la justice et la paix se sont donné un baiser.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
La vérité est sortie de la terre, et la justice a regardé du haut du ciel.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
Le Seigneur accordera sa bonté, et notre terre donnera son fruit.
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
La justice marchera devant lui, et il mettra ses pas dans la voie.