< Masalimo 85 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
to/for to conduct to/for son: descendant/people Korah melody to accept LORD land: country/planet your to return: rescue (captivity *Q(k)*) Jacob
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
to lift: forgive iniquity: crime people your to cover all sin their (Selah)
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
to gather all fury your to return: turn back from burning anger face: anger your
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
to return: again us God salvation our and to break vexation your with us
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
to/for forever: enduring be angry in/on/with us to draw face: anger your to/for generation and generation
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
not you(m. s.) to return: again to live us and people your to rejoice in/on/with you
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
to see: see us LORD kindness your and salvation your to give: give to/for us
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
to hear: hear what? to speak: speak [the] God LORD for to speak: speak peace to(wards) people his and to(wards) pious his and not to return: return to/for confidence
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
surely near to/for afraid his salvation his to/for to dwell glory in/on/with land: country/planet our
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
kindness and truth: faithful to meet righteousness and peace to kiss
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
truth: faithful from land: soil to spring and righteousness from heaven to look
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
also LORD to give: give [the] good and land: country/planet our to give: give crops her
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
righteousness to/for face: before his to go: went and to set: make to/for way: road beat his

< Masalimo 85 >