< Masalimo 85 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
[For the Chief Musician. A Psalm by the sons of Korah.] LORD, you have been favorable to your land. You have restored the fortunes of Jacob.
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
You have forgiven the iniquity of your people. You have covered all their sin. (Selah)
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
You have taken away all your wrath. You have turned from the fierceness of your anger.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Restore us, God of our salvation, and cause your indignation toward us to cease.
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Will you be angry with us forever? Will you draw out your anger to all generations?
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
Won't you revive us again, that your people may rejoice in you?
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
Show us your loving kindness, LORD. Grant us your salvation.
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
I will hear what God, the LORD, will speak, for he will speak peace to his people, his faithful ones; but let them not turn again to folly.
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
Surely his salvation is near those who fear him, that glory may dwell in our land.
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
Mercy and truth meet together. Righteousness and peace have kissed each other.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
Truth springs out of the earth. Righteousness has looked down from heaven.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
Yes, the LORD will give that which is good. Our land will yield its increase.
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
Righteousness goes before him, And prepares the way for his steps.

< Masalimo 85 >