< Masalimo 85 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
To him that excelleth. A Psalme committed to the sonnes of Korah. Lord, thou hast bene fauourable vnto thy land: thou hast brought againe the captiuitie of Iaakob.
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
Thou hast forgiuen the iniquitie of thy people, and couered all their sinnes. (Selah)
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
Thou hast withdrawen all thine anger, and hast turned backe from the fiercenes of thy wrath.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Turne vs, O God of our saluation, and release thine anger toward vs.
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Wilt thou be angry with vs for euer? and wilt thou prolong thy wrath from one generation to another?
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
Wilt thou not turne againe and quicken vs, that thy people may reioyce in thee?
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
Shew vs thy mercie, O Lord, and graunt vs thy saluation.
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
I will hearken what the Lord God will say: for he will speake peace vnto his people, and to his Saintes, that they turne not againe to follie.
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
Surely his saluation is neere to them that feare him, that glory may dwell in our land.
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
Mercie and trueth shall meete: righteousnes and peace shall kisse one another.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
Trueth shall bud out of the earth, and righteousnes shall looke downe from heauen.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
Yea, the Lord shall giue good things, and our land shall giue her increase.
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
Righteousnesse shall go before him, and shall set her steps in the way.