< Masalimo 85 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
For the music director. A psalm of the descendants of Korah Lord, you have shown your kindness to your land; you have restored Jacob's prosperity.
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
You took away your people's guilt; you forgave all their sins. (Selah)
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
You took back your fury; you turned away from your fierce anger.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Bring us back to you, God of our salvation! Take away your anger towards us.
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Are you going to be furious with us forever? Will you stay angry with us for all future generations?
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
Won't you restore our lives so your people can find happiness in you?
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
Show us your trustworthy love, Lord! Give us your salvation!
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
Let me hear what God has to say. God speaks peace to his people, to those who trust in him. But they must not return to their foolish ways.
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
Truly God's salvation is with those who do as he says. His glorious presence will live with us in our land.
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
Trustworthiness and faithful love join together; goodness and peace have kissed each other.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
What is true grows up from the earth; what is right looks down from heaven.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
The Lord will certainly give us all that is good, and our land will produce fine crops.
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
Truth and right go ahead of him to prepare a path for him to walk on.

< Masalimo 85 >