< Masalimo 85 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
Voor muziekbegeleiding. Een psalm van de zonen van Kore. Jahweh, Gij hebt weer uw land begenadigd, En het lot van Jakob ten beste gekeerd;
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
Gij hebt uw volk zijn schuld vergeven, En al zijn zonden bedekt,
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
Heel uw gramschap laten varen, Geblust de gloed van uw toorn.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Richt ons dan op, o God van ons heil, En leg uw wrevel over ons af!
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Of zoudt Gij voor eeuwig op ons vertoornd willen zijn, Verbolgen blijven van geslacht tot geslacht,
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
En niet liever ons laten herleven, Opdat uw volk zich in U kan verheugen?
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
Toon ons uw goedheid, o Jahweh, En schenk ons uw heil!
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
Ik wil horen wat Jahweh mij zegt; Want Hij spreekt woorden van vrede Voor zijn volk en zijn vromen, Voor die op Hem blijven hopen!
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
Waarachtig; zijn heil is nabij aan hen, die Hem vrezen, En zijn heerlijkheid woont in ons Land.
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
Genade en trouw ontmoeten elkander, Gerechtigheid en vrede omhelzen elkaar:
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
De trouw ontspruit aan de aarde, De gerechtigheid blikt uit de hemel.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
Jahweh zelf schenkt zijn zegen, En ons Land geeft zijn oogst;
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
Gerechtigheid gaat voor Hem uit, En geluk volgt zijn schreden!