< Masalimo 85 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
Přednímu z kantorů, synů Chóre, žalm. Laskavěs se, Hospodine, někdy ukazoval k zemi své, přivedls zase z vězení Jákoba.
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
Odpustil jsi nepravost lidu svého, přikryls všeliký hřích jejich. (Sélah)
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
Zdržels všecken hněv svůj, odvrátils od zůřivosti prchlivost svou.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Navratiž se zase k nám, ó Bože spasení našeho, a učiň přítrž hněvu svému proti nám.
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Zdaliž na věky hněvati se budeš na nás? A protáhneš zůřivost svou od národu do pronárodu?
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
Zdaliž ty obrátě se, neobživíš nás, tak aby se lid tvůj veselil v tobě?
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
Ukaž nám, Hospodine, milosrdenství své, a spasení své dej nám.
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
Ale poslechnu, co říká Bůh ten silný, Hospodin. Jistě žeť mluví pokoj k lidu svému, a k svatým svým, než aby se nenavracovali zase k bláznovství.
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
Zajisté žeť jest blízké těm, kteříž se ho bojí, spasení jeho, a přebývati bude sláva v zemi naší.
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
Milosrdenství a víra potkají se spolu, spravedlnost a pokoj dadí sobě políbení.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
Víra z země pučiti se bude, a spravedlnost s nebe vyhlédati.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
Dáť také Hospodin i časné dobré, tak že země naše vydá úrody své.
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
Způsobí to, aby spravedlnost před ním šla, když obrátí k cestě nohy své.