< Masalimo 83 >

1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Ee Mungu, usikae kimya! usitupuuze na kustarehe, Ee Mungu.
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Tazama, adui zako wanafanya vurugu, na wale wakuchukiao wameinua vichwa vyao.
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Wanafanya hila juu ya watu wako na kwa pamoja kupanga njama dhidi ya wale uwalindao. Wamesema,
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
“Njoni na tuwaangamize wao kama taifa. Kisha jina la Israeli halitakumbukwa.”
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Wamepanga njama pamoja wakiwa na mkakati mmoja; wamefanya muungano dhidi yako.
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
Hii inajumuisha hema za Edomu na Waishmaeli, na watu wa Moabu na Wahagari, ambao wamepanga njama pamoja nao
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
Gebal, Amoni, Amaleki; pia inajumuisha Filisti na wenyeji wa Tiro.
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
Ashuri pia ameshirikina nao; wanawasaidia wana wa Lutu. Serah
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Ufanye kwao kama ulivyofanya kwa Midiani, kama ulivyofanya kwa Sisera na kwa Yabini kwenye Mto Kishoni.
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
Waliangamizwa kule Endori na wakawa kama mbolea juu ya chi.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Uvifanye vyeo vyao kama Oreb na Zeeb, na wakuu wao wote kama Zeba na Zalmuna.
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
Wao walisema, natujimilikishe malisho ya Mungu.”
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
Ee Mungu wangu, uwafanye kama mavumbi ya kisulisuli, kama makapi mbele ya upepo,
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
Kama moto uteketezao msitu, na kama miali ya moto iwakayo milimani.
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
Uwafuatie kwa tufani yako, na kuwafadhaisha kwa dhoruba yako.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
Uwajaze nyuso zao kwa aibu ili kwamba waweze kulitafuta jina lako, Yahwe.
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
Nao waaibishwe na kufadhaishwa milele; waangamizwe katika aibu.
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
Kisha watajua kwamba ni wewe pekee, Yahwe, Uliye Juu ya nchi yote.

< Masalimo 83 >