< Masalimo 83 >
1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Oh ʼElohim, no permanezcas en silencio. Oh ʼElohim, no calles, no estés imperturbable.
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Pues [mira que] rugen tus enemigos, Y los que te aborrecen levantan la cabeza.
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Astutamente consultaron contra tu pueblo. Conspiran contra tus protegidos.
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
Dijeron: Vengan. Destruyámoslos para que no sean nación. Que no haya más memoria del nombre de Israel.
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Porque con consentimiento conspiraron juntos. Contra Ti hacen un pacto:
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
Las tiendas de Edom y los ismaelitas, Moab y los agarenos,
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
Gebal, Amón y Amalec, Filistea con los habitantes de Tiro,
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
También Asiria se unió a ellos. Sirven de brazo a los hijos de Lot. (Selah)
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Haz con ellos como con Madián, Como con Sísara, Como con Jabín en el torrente de Cisón,
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
Que fueron destruidos en Endor Y fueron como abono para la tierra.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Haz a sus nobles como a Oreb y a Zeeb, Y a todos sus jefes como a Zeba y Zalmuna,
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
Porque dijeron: Tomemos como posesión nuestra los prados de ʼElohim.
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
Oh ʼElohim mío, conviértelos como un remolino de polvo, Como hojarasca ante el viento,
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
Como fuego que consume el bosque, Como una llama incendia las montañas.
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
Persíguelos así con tu tempestad Y aterrorízalos con tu tormenta.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
Llena sus caras de deshonra, Para que busquen tu Nombre, oh Yavé.
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
Sean avergonzados y turbados para siempre. Sean humillados y perezcan,
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
Y sepan que solo Tú, tu Nombre es Yavé. Eres el ʼElyón sobre toda la tierra.