< Masalimo 83 >

1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Una canción. Un salmo de Asaf. ¡Por favor, no permanezcas en silencio, Dios! ¡No puedes permanecer inmóvil! Dios, ¡No te quedes callado!
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
¿No escuchas el rugido de tus enemigos? ¿No ves cómo los que te odian levantan sus cabezas desafiantemente?
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Inventan planes astutos para conspirar contra tu pueblo; traman cosas contra los que atesoras.
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
Dicen, “¡Vamos! Destruyamos su nación para que el nombre ‘Israel’ sea completamente olvidado”.
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Todos ellos están de acuerdo en su conspiración; han hecho un trato para atacarte—
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
el pueblo de Edom, los Ismaelitas, Moab, y los ismaelitas;
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
el pueblo de Gebal y Ammon y Amalek, Filistea, y los habitantes de Tiro.
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
Asiria también se les ha unido, se ha aliado con los descendientes de Lot. (Selah)
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Hazles lo que le hiciste a Madián, lo que le hiciste a Sisera y Jabin y el río Kishon.
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
Fueron destruidos en Endor y se convirtieron en estiércol para fertilizar la tierra.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Haz a sus líderes como Oreb y Zeeb; todos sus gobernadores como Zeba y Zalmuna,
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
porque ellos dijeron, “¡Tomemos los pastos de Dios para nosotros mismos!”
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
Dios mío, hazlos como torbellinos que giran, como pajas arrasadas por el viento.
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
Como fuego que quema el bosque, como una lama que le prende fuego a las montañas,
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
de la misma forma, derríbalos con tu tormenta, aterrorízalos con tu torbellino.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
¡Avergüénzalos con la derrota para que vengan a ti, Señor!
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
¡Avergüénzalos! ¡Aterrorízalos para siempre, para que mueran en desgracia!
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
Permite que entiendan que solo tú, llamado el Señor, eres el gran Altísimo que rige sobre la tierra.

< Masalimo 83 >