< Masalimo 83 >

1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Ó Deus, não estejas em silencio; não te cales, nem te aquietes, ó Deus.
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Porque eis que teus inimigos fazem tumulto, e os que te aborrecem levantaram a cabeça.
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Tomaram astuto conselho contra o teu povo, e consultavam contra os teus escondidos.
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
Disseram: Vinde, e desarreiguemol-os para que não sejam nação, nem haja mais memoria do nome de Israel.
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Porque consultaram juntos e unanimes; elles se alliam contra ti:
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
As tendas de Edom, e dos ismaelitas, de Moab, e dos agarenos,
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
De Gebal, e de Ammon, e de Amalek, de Palestina, com os moradores de Tyro.
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
Tambem Assyria se ajuntou com elles: foram ajudar aos filhos de Lot (Selah)
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Faze-lhes como aos madianitas; como a Sisera, como a Jabin na ribeira de Kison.
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
Os quaes pereceram em Endor; tornaram-se como estrume para a terra.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Faze aos seus nobres como a Oreb, e como a Zeeb e a todos os seus principes, como a Zebah e como a Zalmuna;
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
Que disseram: Tomemos para nós as casas de Deus em possessão.
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
Deus meu, faze-os como um tufão, como a aresta diante do vento.
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
Como o fogo que queima um bosque, e como a chamma que incendeia as brenhas,
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
Assim os persegue com a tua tempestade, e os assombra com o teu torvelinho.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
Encham-se de vergonha as suas faces, para que busquem o teu nome, Senhor.
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
Confundam-se e assombrem-se perpetuamente; envergonhem-se, e pereçam.
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
Para que saibam que tu, a quem só pertence o nome de Jehovah, és o Altissimo sobre toda a terra.

< Masalimo 83 >